Isaiah 23

Za Chilango cha Turo

1Uthenga wonena za Turo:

Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi:
pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa
ndipo mulibe nyumba kapena dooko.
Zimenezi anazimva
pochokera ku Kitimu.

2Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja,
inu amalonda a ku Sidoni,
iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
3Pa nyanja zazikulu
panabwera tirigu wa ku Sihori;
zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda
ndi anthu a mitundu ina.

4Chita manyazi, iwe Sidimu
pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti,
“Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana;
sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
5Mawuwa akadzamveka ku Igupto,
iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.

6Wolokerani ku Tarisisi,
lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
7Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja,
mzinda wakalekale,
umene anthu ake ankapita
kukakhala ku mayiko akutali?
8Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina,
mzinda umene amalonda ake ndi akalonga
ndi otchuka
pa dziko lapansi?
9Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi
kuti athetse kunyada kwawo
ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.

10Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo
inu anthu a ku Tarisisi,
pakuti mulibenso chokutetezani.
11Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja
ndipo wagwedeza maufumu ake.
Iye walamula kuti Kanaani
agwetse malinga ake.
12Iye anati, “Simudzakondwanso konse,
inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa!

“Ngakhale muwolokere ku Kitimu,
kumeneko simukapezako mpumulo.”
13Onani dziko la Ababuloni,
anthu amenewa tsopano atheratu!
Asiriya asandutsa Turo kukhala
malo a zirombo za ku chipululu;
anamanga nsanja zawo za nkhondo,
anagumula malinga ake
ndipo anawasandutsa bwinja.

14Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi;
chifukwa malinga ako agwetsedwa!
15Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:

16“Tenga zeze wako uzungulire mzinda,
iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika;
imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri,
kuti anthu akukumbukire.”
17Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi. 18Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.

Copyright information for NyaCCL